Mutikhululukile Ambuye ndife OchimwA
Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Mutikhululukile Ambuye ndife OchimwA, Health/Beauty, WhatsApp number +256994278444, Mulanje.
Buku Lopatulika
Genesis 6:1-3 Ndipo panali pamene anthu anayamba kucuruka padziko, ndi ana akazi anawabadwira iwo, kuti ana amuna a Mulungu anayang'ana ana akazi a anthu, kuti iwo anali okongola; ndipo anadzitengera okha akazi onse amene anawasankha. Ndipo anati Yehova, Mzimu wanga sudzakangana ndi anthu nthawi zonse, cifukwa iwonso ndiwo thupi lanyama: koma masiku ace adzakhala zaka zana limodzi kudza makumi awiri.
WA MAU A MULUNGU PA MOYO WATHU πβοΈ
:23-24 ππΉβοΈ
π£οΈNdipo tsopano, cotsani milungu yacilendo iri pakati pa inu, ndi kulozetsa mitima yanu kwa Yehova, Mulungu wa Israyeli. Ndipo anthu anati kwa Yoswa, Tidzamtumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera mau ace.
πΉβοΈ Okondedwa azanga apaulendo mau awa akulankhura ndi Mulungu kudzera mwa Yoswa kulankhura ndi ana a lsrayeri zokhudza kuchotsa milungu yachilendo pakati pao, mau awa tikuwapeza pamene Yoswa akubweleza kucita pangano pakati anthu ndi Mulungu, ndipo tikumva ana a lsrayeri akulonjeza kusatumikira milungu ina koma Yehova yekha, ndipo Yoswa akuwacenjezaso kuti ngati mwabvomekeza kutero chotsani milungu yonse pakati panu ndi kusankha Yehova Mulungu yekha, tikuyenera kuchotsa tchimo pakati pathu π.
πΉβοΈ Okondedwa azanga apaulendo, Mulungu akulankhura ndi moyo wathu lero zakuchotsa milungu yachilendo pakati pathu, ngati tabvomera kuntumikira lye yekha tichotse tchimo pa moyo wathu ndikuika mtima wathu pa lye yekha, Mulungu atalankhura kudzera mwa Yoswa ana a lsrayeri anamvomera kuchotsa tchimo pakati pao, m'bale or m'longo mau awa lero ndi athu Mulungu akulankhura ndi moyo wathu, Yoswa akulankhura ndi moyo wathu zakuchotsa milungu yachilendo (tchimo ) pakati pathu tiyeni tibvomere monga lsrayeri pakulapa tchimo lathu lero, tiyeni tifewetse khosi mtima wathu pamene talankhulidwa talalikidwa taphuzitsidwa ndi kulapa tchimo lathu, tiyeni tikonze moyo wathu lero pakulapa tchimo, tiyeni tichotse milungu yachilendo pakati pathu kuti Mulungu atsekure njira zathu ndi kuika chipambano pa moyo wathu. Ambuye Akudalitseni ndi kulenga chatsopano mwa inu. β
Mulungu akudalitseni nonse amene mumatenga nawo mbari pa page imeneyi ambuye asinthe nyengo zanu
Mateyu 11:28 Idzani kuno kwa Ine nonsenu akulema ndi akuthodwa, ndipo Ine ndidzakupumulitsani inu.
Tumizani # yanu tikupangeni add ku group lathu la WhatsApp
08/05/2024
04/05/2024
Group ija ndimene mukuiwonayo ππππππππ
MUTIKHULULUKIRE AMBUYE Ndife OCHIMWA
Group online WhatsApp inbox me 0994278444
Mutikhululukire ambuye ndife ochimwa group lija lapangidwa ku WhatsApp tumizani number yanu kuti tikupangeni add ndicholinga choti mukhale nawo mugulu lolandira nawo mauthenga okutengerani kwa yesu khristu
Ambuye akudaliseni shalom shalom shalom
YOHANE 12vs 24 mpka 30 Indetu, Indetu, ndinena ndi inu, ngati mbeu ya tirigu siigwa m'nthaka, nifa, ikhala pa yokha uyo; koma ngati ifa, ibara cipatso cambiri. Moyo wanga wabvutika tsopano; ndipo ndidzanena ciani? Atate, ndipulumutseni ine ku nthawi iyi. Kom Cifukwa ca ici ndinadzera nthawi iyi. Atate, lemekezani dzina lanu, pomwepo adadza mau ocokera kumwamba, ndalilemekeza ndipo ndidzalilemekezanso. Cifukwa cace khamu la anthu akuimirirako, ndi kuwamva ananena kuti kwagunda. Ena ananena, Mngero walankhula ndi iye. yesu anayankha nati, Mau awa sanafika cifukwa ca ine, koma ca inu, okondedwa mulungu ndiwachifundo mulungu alibe tsankhu ndipo athu ena amati ineyo mulungu salakhula nane ai ai okondedwa mulungu amalakhula ndi aliyese kungoti inu simudziwa lelo ndiwani kuti mulungu walankhula nanu) chisomo chachikulu chinachitika kare kunakhala ndi kwamuthu kuvomereza kuti yesu ndi ambuye waona iye waona mulungu palibe amene amafika kwa mulungu osalumikizana ndi yesu mpulumutsi MASALMO 118vs 19.20) nditsegulireni zipata za cilungamo, ndidzayamika yehova. Cipata ca yehova ndi ici; Olungama adzalowamo. Abare dziwani ici pa maola 24 pansi pano athu omwalila ndi masauzande ambili koma kumwamba tsiku limatha thawi zina osalowako muthu pena modzi penaso awili atatu koma kumwamba kumakhala chimwemwe kwambili cifukwa ca muthu modzi pena atatuwo ndipo ambuye yesu amati wacita bwino mwana wanga) koma taonani tchimo libara ifa tifelanji ife thawi yathu isanakwane thawi ino tiyeni abare tizipempha zisomo za cipulumutso zitigwere
Pangani like follow and shere page kuti tipitilize kufalisa uthenga wabwino wa ambuye yesu khristu
Ambuye akudaliseni shalom shalom shalom shalom
Click here to claim your Sponsored Listing.
Category
Website
Address
Mulanje
